Ask AI
Integrating PrEP to End HIV
Thanzi la Amayi Ndi Thanzi la Dera Lonse: Kuphatikiza PrEP mu Zithandizo za ku Dera Kuti Tithetse HIV

Released: March 02, 2026

Activity

Progress
1
Course Completed
Key Takeaways
  • Kuphatikiza njira zopewera kachirombo ka HIV ndi zithandizo za kudera kumabweretsa zabwino zambiri kuposa munthu payekha.
  • Kuphatikiza bwino kwa PrEP kumafuna maphunziro a HCP poyambirira, kugwira ntchito ndi anthu a ku dera, komanso kuyika ndalama mosadukiza kuti anthu akhale ndi mwayi wosankha njira zenizeni zopewera HIV.

Ndiyambe ndi nkhani ya zaka zambiri zapitazo, chipatala chathu chisanayambe kuyeza ndi kupewa HIV m’zithandizo za amayi oyembekezera. Mayi wina adabwera ku chipatala changa ndipo adandiuza kuti adapezeka ndi kachirombo ka HIV. Iye adati, “Ndidabereka komaliza kuno zaka ziwiri zapitazo, ndipo palibe amene adandiuzako zokhudza HIV.” Palibe amene adandiuza kuti ndidali pa chiwopsezo. Ndine wokwatiwa. Ndinkaganiza kuti ndidali bwino. Palibe amene adalankhula nane.” Tidamulakwitsa ndife. Ndonomeko zidamulakwitsa. Ngati tikufuna kupewa zinthu ngati zomwe zidamuchitikira iyeyu, tikuyenera kuphatikiza njira zopewera kufala kwa matendawa (PrEP) ndi chisamaliro cha amayi chachikhalidwe.

HIV ndi Mliri wa Amayi
Kuphatikiza PrEP mu zithandizo za kudera, monga kulera ndi ntchito zaumoyo wa amayi ndi ana, zikuwoneka ngati njira yosavuta kuthandizira kupewa HIV ku sub-Saharan Africa, chifukwa kuno mliriwu ndi mliri wa amayi. Chiwerengero chachikulu cha anthu omwe ali ndi kachirombo ka HIV m'derali chili pakati pa amayi achichepere azaka zapakati pa 15 ndi 24. Ngakhale zina mwa izi ndi kaamba ka kapangidwe ka thupi la mkazi, zochitika pakati pa anthu nazonso zimatengapo gawo.

Chiwopsezo chachikulu cha kufalikira kwa kachirombo ka HIV ndi kuchuluka kwa tizilombo ta HIV m'dera, kapena kuchuluka kwa anthu omwe ali ndi kachilombo ka HIV m'dera la munthu. Ngakhale munthu atakhala ndi wachikondi m'modzi, ngati kufalikira kwa kachirombo ka HIV kuli 20% m’deralo, m’modzi (1) mwa anthu asanu (5) alionse akhoza kukhala ndi kachirombo ka HIV.

Kuphatikiza PrEP mu Chisamaliro cha Umoyo wa Amayi
Posatengera kuti chiwerengero cha kachirombo ka HIV ndichochuluka m'madera amenewa, ndapeza kuti amayi ambiri achichepere amaopa kwambiri kutenga mimba kuposa kachirombo ka HIV. Choncho, ngati akatswiri azaumoyo (HCPs) akufuna kukumana ndi mzimayi wachichepere yemwe ali pachiwopsezo pa nthawi yomwe akufunika thandizo, kuphatikiza chisamaliro cha HIV ndi njira zolerera komanso chisamaliro cha kugonana kuyenera kukhala patsogolo pathu.

Ndikuganiza kuti imodzi mwa mfundo zazikulu kwambiri zokhudzana ndi kuphatikiza kwa PrEP idali mayeso a ECHO, yomwe idawunika ngati njira zina zolerera zimagwirizana ndi kuwonjezera chiopsezo chotenga kachirombo ka HIV.

Panalibe kusiyana kulikonse pakati pa kuchuluka kwa kachirombo ka HIV pakati pa njira zirizonse zolerera zomwe zinayesedwa, koma ofufuza adanena kuti kuchuluka kwa kachirombo ka HIV pakati pa amayi achichepere omwe adatenga mbali pa kafukufukuyu kunali kwakukulu kwambiri. Tangoganizirani ngati amayi omwe amagwiritsa ntchito njira zakulera ankagwiritsanso ntchito PrEP. Kodi zimenezi zikadathandiza kupewa kufala kwa HIV kochuluka bwanji?

Kupewa kachirombo ka HIV msanga kungakhale ndi zotsatira zokhalitsa. Pamene mzimayi wopanda kachirombo ka HIV walowa m’banja, mwamuna wake nayenso amakhalabe wopanda kachirombo ka HIV, komanso ana ake, zomwe zimachepetsa chiwopsezo chawo cha matenda ena okhudzana ndi kachirombo ka HIV, monga khansa ya Kaposi ndi khansa ya khomo la chiberekero. Choncho kuphatikiza PrEP mu zithandizo za ku madera kungakhale ndi phindu lenileni kwa anthu aku dera.

Kupanga Zinthu Zothandiza Pophatikiza PrEP
Gawo lofunika kwambiri ndi kuphatikiza maphunziro okhudza kupewa kachirombo ka HIV komanso chithandizo m’maphunziro a za umoyo a uchembere. Ngati kupewa kachirombo ka HIV kungaphatikizidwe koyambirira pa nthawi yophunzitsa akatswiri a zaumoyo, chimakhala chithandizo chosavuta kupereka.

Kusalana kaamba ka HIV kukanali kochuluka m'chigawo changa. Kotero, ine ndi anzanga tidayesetsa kuyambitsa kuyezetsa HIV ndi PrEP m'zithandizo za anthu ochotsa mimba chifukwa kuchotsa mimba kumasalidwanso ndikale. Azimayi omwe adachotsa kale mimba amakhala ndi kuthekera kochotsa mimba mobwerezabwereza, kusonyeza chiwopsezo chopitilira komanso kugonana mosadziteteza.

Mu kafukufuku wofufuza kuyambitsa PrEP ku chithandizo cha amayi omwe achotsa mimba, chotchinga chachikulu pa kupereka PrEP chinali kuchepa kwa chidziwitso cha kupewa HIV komanso kusasangalatsidwa kuyezedwa HIV pakati pa akatswiri azaumoyo omwe ali pamsinkhu wobereka. M'zipatala, komwe atsogoleri amagulu adalimbikitsa kuphatikiza zithandizo zopewera HIV kuphatikizapo PrEP, kugwiritsa ntchito mankhwala kunali kwakukulu komanso kuyamba kugwiritsa ntchito njira yophatikizira kunali kosavuta.

Malangizo anga pakuphatikiza bwino chisamaliro komanso kupewa HIV kuli m’magawo atatu (3). Choyamba, muyenera kugwira ntchito ndi akatswiri anu azaumoyo. Muyenera kumvetsetsa tsankho lawo ndikuwathandiza kuthetsa kusalana kokhudzana ndi kachilombo ka HIV.

Chachiwiri, muyenera kumvetsetsa dera lanu. Muyenera kuyankhula ndi atsogoleri ofunikira poyambirira. Atsogoleri achipembedzo komanso malo omwe amakumana zingathandizire kusalidwa kwa amayi pankhani zogonana. Ngati sitigwiritsa ntchito malo amenewa, zidzakhala cholepheretsa kuti anthu azigwiritse ntchito. Tikhoza kupeza njira zabwino kwambiri, zotetezeka, zotsika mtengo, koma ngati anthu akudera sali omasuka kuzigwiritsa ntchito, kufikira anthu ochuluka sikungatheke.

Chachitatu, muyenera kudziwa ndalama zomwe zikufunika kuti mufikire anthu omwe ali pa chipsinjo chopezeka ndi kachirombo ka HIV. Nthawi zambiri, omwe timathandizana nawo amabwera ndi zinthu koma opanda njira zothandizira kuti zigwiritsidwe ntchito. Tikufunika kuthandizira zokambirana ndi anthu a ku dera komanso kugwira ntchito ndi anthu ofunikira, komanso maphunziro amnsanga kwa ogwira ntchito za umoyo.

Chisankho Ndi Mphamvu
Pomaliza pake, ngati sitipereka mwayi kwa amayi kuti adziteteze ku HIV, tikuwalakwira. 

Ndidayamba ndi nkhani ya mzimayi amene tidamulakwira. Nkhani imeneyi imandikhudza kwambiri. Adabwera kwa ife chifukwa cha mimba yake koma ife sitinathane ndi chiwopsezo cha kutsogolo kwake chotenga kachirombo ka HIV. Tyeni tisasemphane ndi miyayi imeneyi.

Maganizo Anu
Ndi njira ziti zomwe mungagwiritse ntchito kuti muphatikize chisamaliro ndi kupewa HIV mu ntchito yanu? Perekani ndemanga kuti mulowe nawo mu zokambirana!